7 Ndipo anadza nane ku cipata ca kubwalo, ndipo popenya ine, taonani, pobooka palinga.
8 Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, booletsa kulinga; ndipo nditabooletsa palinga, ndinaona khomo.
9 Ndipo anati kwa ine, Lowa, kapenye zonyansa zoipa alikuzicita komweko.
10 M'mwemo ndinalowa ndi kupenya, ndipo taonani, maonekedwe ali onse a zokwawa, ndi zirombo zonyansa, ndi mafano onse a nyumba ya Israyeli, zolembedwa pakhoma pozungulira ponse.
11 Ndipo pamaso pao panaima amuna makumi asanu ndi awiri a akulu a nyumba ya Israyeli, ndi pakati pao panaima Jazaniya mwana wa Safana munthu ali yense ndi mbale yace ya zofukiza m'dzanja lace; ndi pfungo lace la mtambo wa zonunkhira linakwera.
12 Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, wapenya kodi cocita akulu a nyumba ya lsrayeli mumdima, ali yense m'cipinda cace ca zifanizo? pakuti ati, Yehova satipenya, Yehova wataya dziko.
13 Anatinso kwa ine, Udzaonanso zonyansa zazikuru zina azicita.