6 Pamaso pao uwasenze paphewa pako, ndi kuwaturutsa kuli mdima, nuphimbe nkhope yako kuti usapenye dziko; popeza ndakuika cizindikilo ca nyumba ya Israyeli.
7 Ndipo ndinacita monga momwe anandilamulira, ndinaturutsa akatundu anga usana, ngati a pa ulendo wa kundende, ndi madzulo ndinaboola pakhoma ndi dzanja langa, ndinawaturutsa pali mdima, ndi kuwasenza paphewa panga pamaso: pao.
8 Ndipo m'mawa mau a Yehova anandidzera, ndi kuti,
9 Wobadwa ndi munthu iwe, kodi nyumba ya Israyeli, nyumba yampanduko, siinati kwa iwe. Ucitanji?
10 Unene nao, Atero Ambuye Yehova, Katundu uyu anena za kalonga wa m'Yerusalemu, ndi nyumba yonse ya Israyeli yokhala pakati pao.
11 Uziti, Ine ndine cizindikilo canu, monga ndacita ine momwemo kudzacitidwa nao; adzacotsedwa kumka kundende.
12 Kalongayo ali pakati pao adzasenza paphewa pace mumdima, nadzaturuka; adzaboola palinga, nadzaturutsapo; adzaphimba nkhope yace kuti asapenye dziko ndi maso ace.