22 Nnena cimodzi conse ca zolakwa zace zonse adazicita cidzakumbukika cimtsutse; m'cilungamo cace adacicita adakhala ndi moyo.
23 Ngati ndikondwera nayo imfa ya woipa? ati Ambuye Yehova, si ndiko kuti abwerere kuleka njira yace, ndi kukhala ndi moyo?
24 Koma wolungamayo akabwerera kuleka cilungamo cace, nakacita mphulupulu, ndi kucita monga mwa zonyansa zonse azicita woipa, adzakhala ndi moyo kodi? Nnena cimodzi ca zolungama zace zonse adzazicita cidzakumbukika m'kulakwa kwace analakwa nako, ndi m'kucimwa kwace anacimwa nako; momwemo adzafa.
25 Koma mukuti, Njira ya Ambuye njosayenera. Tamvera tsono nyumba ya Israyeli, Kodi njira yanga njosayenera? njira zanu si ndizo zosayenera?
26 Wolungamayo akatembenukira kuleka cilungamo cace, nakacita mphulupulu, adzafa momwemo; m'mphulupulu yace adaicita adzafa.
27 Ndipo woipayo akatembenukira kuleka coipa cace adacicita, nakacita ciweruzo ndi cilungamo, adzapulumutsa moyo wace.
28 Popeza anasamalira, natembenukira kuleka zolakwa zace zonse adazicita, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.