4 Mitundu ya anthu idamva mbiri yace, unagwidwa m'mbuna mwao; ndipo anadza nao ndi zokowera ku dziko la Aigupto.
5 Pakuona tsono waukaziwo, kuti unalindirira, ndi kuti ciyembekezo cace cidatha, unatenga wina wa ana ace, numsandutsa msona.
6 Ndipo unayendayenda pakati pa mikango, nukhala msona, nuphunzira kugwira nyama, nulusira anthu.
7 Ndipo unadziwa amasiye ao, nupasula midzi yao, ndipo dziko ndi kudzala kwace linasanduka labwinja, cifukwa ca phokoso la kubangula kwace.
8 Pamenepo mitundu ya anthu inadzipereka kuukola kucokera ku maiko a ku mbali zonse, niuphimba ndi ukonde wao, nugwidwa uwu m'mbuna mwao.
9 Nauika m'citatanga ndi zokowera, nadza nao kwa mfumu ya ku Babulo; anaulonga m'malinga, kuti mau ace asamvekenso pa mapiri a Israyeli.
10 Mai wako ananga mpesa wookedwa kumadzi; muja anakhala mumtendere unabala zipatso, wodzala ndi nthambi, cifukwa ca madzi ambiri.