18 Ndipo ndinati kwa ana ao m'cipululu, Musamayenda m'malemba a atate anu, musawasunga maweruzo ao, kapena kudzidetsa ndi mafano ao;
19 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, muziyenda m'malemba anga, ndi kusunga maweruzo anga, ndi kuwacita;
20 muzipatulanso masabata anga, ndipo adzakhala cizindikilo pakati pa Ine ndi inu, kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
21 Koma anawo anapandukira Ine, sanayenda m'malemba anga, kapena kusunga maweruzo anga kuwacita, amene munthu akawacita adzakhala nao ndi moyo; anaipsa masabata anga; pamenepo ndinati ndidzawatsanulira ukali wanga, kuwakwaniritsira mkwiyo wanga m'cipululu.
22 Koma ndinabweza dzanja langa ndi kucicita, cifukwa ca dzina langa; kuti lisaipsidwe pamaso pa amitundu, amene ndinawaturutsa pamaso pao. Ndinawakwezeranso dzanja langa m'cipululu,
23 kuti ndidzawabalalitsa mwa amitundu, ndi kuwamwaza m'maiko;
24 popeza sanacita maweruzo anga, koma ananyoza malemba anga, naipsa masabata anga, ndi maso ao anatsata mafano a atate ao.