15 Anthu a ku Dedani anakutsatsa malonda, zisumbu zambiri zinazolowerana nawe malonda ako, anabwera nazo minyanga ndi phingo kugulana nawe malonda.
16 Aramu anacita nawe malonda cifukwa ca zambirizo udazipanga, anagula malonda ako ndi smaragido, nsaru yofiirira, ndi yopikapika, ndi bafuta, ndi korale, ndi ngale.
17 Yuda ndi dziko la Israyeli anagulana nawe malonda, anagula malonda ako ndi tirigu wa ku Miniti, ndi zozuna, ndi uci, ndi mafuta, ndi mafuta amankhwala.
18 Damasiko anagulana nawe malonda cifukwa ca zambirizo udazipanga, cifukwa ca kucuruka kwa cuma ciri conse, ndi vinyo wa ku Keliboni, ndi ubweya wa nkhosa woyera.
19 Vedani ndi Yavani anagula malonda ako ndi thonje, unagulana nao citsulo cosalala, ngaho, ndi mzimbe.
20 Dedani anagulana nawe malonda ndi nsaru za mtengo wace zoyenda nazo pa kavalo.
21 Arabu ndi akalonga onse a ku Kedara anazolowerana nao malonda ako; ana a nkhosa, nkhosa zamphongo, ndi mbuzi, izi anagulana nawe.