3 nena, uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona nditsutsana nawe, Farao mfumu ya Aigupto, ng'ona yaikuru yakugona m'kati mwa mitsinje yace, imene ikuti, Mtsinje wanga ndi wangatu, ndadzipangira ndekha uwu.
4 Koma ndidzaika mbedza m'kamwa mwako, ndi kumamatiritsa nsomba za m'mitsinje mwako ku mamba ako; ndipo ndidzakukweza kukuturutsa m'kati mwa mitsinje yako, pamodzi ndi nsomba zonse za m'mitsinje mwako zomamatira pa mamba ako.
5 Ndipo ndidzakutaya kucipululu, iwe ndi nsomba zonse za m'mitsinje mwako; udzagwa kuthengo koyera, sudzaunjikidwa, kapena kuoledwa; ndakupereka ukhale cakudya ca zirombo za padziko, ndi mbalame za kumlengalenga,
6 Ndi onse okhala m'Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, popeza anakhalira nyumba ya Israyeli mcirikizo wabango.
7 Muja anakugwira ndi dzanja unatyoka, ndi kulasa mapewa ao onse; ndi muja anakutsamira unatyoka, ndi kuwagwedeza ziuno zao zonse.
8 Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Taona, ndikudzera ndi lupanga, ndi kukulikhira munthu ndi nyama.
9 Ndi dziko la Aigupto lidzakhala lopasuka ndi labwinja; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, popeza anati, Mtsinjewo ndi wanga, ndinaulenga ndine.