30 Ndipo panali atatha Isake kumdalitsa Yakobo, ataturuka Yakobo pamaso pa Isake atate wace, Esau mkuru wace analowa kucokera kuthengo,
31 Ndipo iyenso anakonza cakudya cokolera, nadza naco kwa atate wace, nati kwa atate wace, Auke atate wanga, adye nyama ya mwana wace, kuti moyo wanu undidalitse ine.
32 Ndipo Isake atate wace anati kwa iye, Ndiwe yani? ndipo iye anati, Ndine mwana wanu woyamba Esau.
33 Ndipo Isake ananthunthumira ndi kunthunthumira kwakukuru, nati, Ndani uja anatenga nyama, nadza nayo kwa ine, ndipo ndadyako zonse usadaloweiwe, ndipondamdalitsaiye? inde, adzadalitsika.
34 Pamene Esau anamva mau a atate wace Isake, analira ndi kulira kwakukuru ndi kowawa kopambana, nati kwa atate wace, Mundidalitse ine, inenso atate wanga.
35 Ndipo iye anati, Mphwako anadza monyenga, nalanda mdalitso wako.
36 Ndipo iye anati, Kodi si ndico cifukwa anamucha dzina lace Yakobo? kuti wandinyenga ine kawiri aka; analanda ukulu wanga ndipo taonani, tsopano walanda mdalitso wanga. Ndipo anati, Kodi smunandisungira ine mdalitso?