1 Tamvani mau amene Yehova anena kwa inu, nyumba ya Israyeli;
2 atero Yehova, a Musaphunzire njira ya amitundu, musaope zizindikiro za m'thambo; pakuti amitundu aziopa izo.
3 Pakuti miyambo ya anthu iri yacabe, pakuti wina adula mtengo m'nkhalango, nchito ya manja a mmisiri ndinkhwangwa.
4 Aukometsa ndi siliva ndi golidi; aucirikiza ndi misomali ndi nyundo, kuti usasunthike.