19 Farao mfumu ya ku Aigupto, ndi atumiki ace, ndi akuru ace, ndi anthu ace onse;
20 ndi anthu onse osanganizidwa, ndi mafumu onse a dziko la Uzi, ndi mafumu onse a dziko la Afilisti, ndi Asikeloni, ndi Gaza, ndi Ekroni, ndi otsala a Asdodi,
21 Edomu, ndi Moabu, ndi ana a Amoni,
22 ndi mafumu onse a Turo, ndi mafumu onse a Zidoni, ndi mafumu a cisumbu cimene ciri patsidya pa nyanja;
23 Dedani, ndi Tema, ndi Buzi, ndi onse amene ameta m'mbali mwa tsitsi;
24 ndi mafumu onse a Arabiya, ndi mafumu onse a anthu osanganizidwa okhala m'cipululu;
25 ndi mafumu onse a Zimiri, ndi mafumu onse a Elamu, ndi mafumu onse a Medi,