2 Koma ngakhale iye, ngakhale atumiki ace, ngakhale anthu a padziko, sanamvere mau a Yehova, amene ananena mwa Yeremiya mneneri.
3 Ndipo Zedekiya mfumu anatuma Yehukali mwana wa Selemiya, ndi Zefaniya mwana wa Maseya wansembe, kwa Yeremiya mneneri, kukanena, Mutipemphereretu kwa Yehova Mulungu wathu.
4 Ndipo Yeremiya analikuyendayenda mwa anthu; cifukwa asanamuike iye m'nyumba yandende.
5 Ndipo nkhondo ya Farao inaturuka m'Aigupto; ndipo pamene Akasidi omangira misasa Yerusalemu anamva mbiri yao, anacoka ku Yerusalemu.
6 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya mneneri, kuti,
7 Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli: Muzitero kwa mfumu ya Yuda, imene inakutumani inu kwa Ine kuti mundifunse Ine: Taonani, nkhondo ya Farao, yakuturukira kudzathandiza inu, idzabwerera ku Aigupto ku dziko lao.
8 Ndipo Akasidi adzabweranso, nadzamenyana ndi mudzi uwu; ndipo adzaulanda, nadzautentha ndi moto.