10 Ndipo Ismayeli anatenga ndende otsala onse a anthu okhala m'Mizipa, ana akazi a mfumu, ndi-anthu onse amene anatsala m'Mizipa, amene Nebuzaradani kapitao wa alonda anapatsira Gedaliya mwana wa Ahikamu; Ismayeli mwana wa Netaniya anawatenga ndende, napita kukaolokera kwa ana a Amoni.