31 Ndipo panali caka ca makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri ca undende wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda, mwezi wakhumi ndi iwiri, tsiku la makumi awiri ndi asanu la mwezi, Evili-Merodaki mfumu ya ku Babulo anaweramutsa mutu wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda, namturutsa iye m'ndende;