5 Ndipo ndidzayesa Raba khola la ngamira, ndi ana a Amoni popumula zoweta zazing'ono; matero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 Pakuti atero Ambuye Yehova, Waomba manja, ndi kubvina, ndi kukondwera ndi cipeputso conse ca moyo wako, kupeputsa dziko la Israyeli,
7 cikufwa cace taona, ndakutambasulira dzanja langa, ndipo ndidzakupereka ukhale cofunkha ca amitundu, ndi kukudula mwa mitundu ya anthu, ndi kukutayikitsa m'maiko, ndidzakuononga; motero udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
8 Atero Ambuye Yehova, Popeza Moabu ndi Seiri akuti, Taona nyumba ya Yuda ikunga amitundu onse;
9 cifukwa cace taona, ndidzatsegula pambali pace pa Moabu kuyambira ku midzi, ku midzi yace yokhala mphepete, yokometsetsa ya m'dziko, Betiyesimoti, Baalameoni, ndi Kiriataimu,
10 kuwapereka kwa ana a kum'mawa pamodzi ndi ana a Amoni; ndipo ndidzawapereka akhale ao ao, kuti ana a Amoni asakumbukikenso mwa amitundu;
11 ndipo ndidzakwaniritsa maweruzo m'Moabu; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.