4 Koma ndidzaika mbedza m'kamwa mwako, ndi kumamatiritsa nsomba za m'mitsinje mwako ku mamba ako; ndipo ndidzakukweza kukuturutsa m'kati mwa mitsinje yako, pamodzi ndi nsomba zonse za m'mitsinje mwako zomamatira pa mamba ako.
5 Ndipo ndidzakutaya kucipululu, iwe ndi nsomba zonse za m'mitsinje mwako; udzagwa kuthengo koyera, sudzaunjikidwa, kapena kuoledwa; ndakupereka ukhale cakudya ca zirombo za padziko, ndi mbalame za kumlengalenga,
6 Ndi onse okhala m'Aigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, popeza anakhalira nyumba ya Israyeli mcirikizo wabango.
7 Muja anakugwira ndi dzanja unatyoka, ndi kulasa mapewa ao onse; ndi muja anakutsamira unatyoka, ndi kuwagwedeza ziuno zao zonse.
8 Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Taona, ndikudzera ndi lupanga, ndi kukulikhira munthu ndi nyama.
9 Ndi dziko la Aigupto lidzakhala lopasuka ndi labwinja; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, popeza anati, Mtsinjewo ndi wanga, ndinaulenga ndine.
10 Cifukwa cace taona, nditsutsana ndi iwe ndi mitsinje yako, ndipo ndidzasandutsa dziko la Aigupto likhale lopasuka konse, ndi labwinja, kuyambira nsanja ya Sevene kufikira malire a Kusi.