24 Cifukwa cace ndidzabalalitsa iwo, monga ziputu zakupita, ndi mphepo ya kucipululu.
25 Ici ndi cagwera cako, gawo la muyeso wako wa kwa Ine, ati Yehova; cifukwa wandiiwala Ine, ndi kukhulupirira zonama.
26 Cifukwa cace Ine ndidzaonetsa zotopola mikawo zako, pamaso pako, ndipo manyazi ako adzaoneka.
27 Ndaona zonyansa zako, ndi zigololo zako, ndi zakumemesa zako, ndi cinyerinyeri ca dama lako, pamapiri ndi m'munda. Tsoka kwa iwe, Yerusalemu! Sudzayeretsedwa; kodi zidzatero mpaka liti?