11 Kodi mtundu wa anthu unasintha milungu yao, imene siiri milungu? Koma anthu anga anasintha ulemerero wao ndi cosapindula.
12 Muzizwe pamenepo, miyamba inu, muope kwambiri, mukhale ouma, ati Yehova.
13 Pakuti anthu anga anacita zoipa ziwiri; anandisiya Ine kasupe wa madzi amoyo, nadziboolera zitsime, zitsime zong'aluka, zosakhalamo madzi.
14 Kodi Israyeli ndi mtumiki? kodi ndiye kapolo wobadwa m'nyumba? afunkhidwa bwanji?
15 Ana a mikango anambangulira iye, nakweza mau; anapasula dziko lace, midzi yace yatenthedwa, mulibenso wokhalamo.
16 Ananso a Nofi ndi a Tahapanesi, anaswa pakati pamtu pako.
17 Kodi sunadzicitira ici iwe wekha popeza unasiya Yehova Mulungu wako, pamene anatsogolera iwe panjira?