37 Uzitero kwa mneneri, Yehova wakuyankha ciani? ndipo Yehova wanenanji?
38 Koma ngati muti, Katundu wa Yehova, cifukwa cace Yehova atero: Cifukwa muti mau awa, Katundu wa Yehova, ndipo ndatuma kwa inu, kuti, Musati, Katundu wa Yehova;
39 cifukwa cace, taonani, ndidzakuiwalani inu konse, ndipo ndidzakucotsani, ndi mudzi umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu, ndidzaucotsa pamaso panga;
40 ndipo ndidzakutengerani inu citonzo camuyaya, ndi manyazi amuyaya, amene sadzaiwalika.