21 Edomu, ndi Moabu, ndi ana a Amoni,
22 ndi mafumu onse a Turo, ndi mafumu onse a Zidoni, ndi mafumu a cisumbu cimene ciri patsidya pa nyanja;
23 Dedani, ndi Tema, ndi Buzi, ndi onse amene ameta m'mbali mwa tsitsi;
24 ndi mafumu onse a Arabiya, ndi mafumu onse a anthu osanganizidwa okhala m'cipululu;
25 ndi mafumu onse a Zimiri, ndi mafumu onse a Elamu, ndi mafumu onse a Medi,
26 ndi mafumu onse a kumpoto, a kutari ndi a kufupi, wina ndi mnzace; ndi maufumu onse a dziko lapansi, okhala pansi pano; ndi mfumu ya Sesaki adzamwa pambuyo pao.
27 Ndipo uziti kwa iwo, Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Imwani inu, ndi kuledzera, ndi kusanza, ndi kugwa, osanyamukanso konse, cifukwa ca lupanga limene ndidzatumiza mwa inu.