2 Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, kuti, Ndatyola gori la mfumu ya ku Babulo.
3 Zisanapite zaka ziwiri zamphumphu Ine ndidzabwezeranso kumalo kuno zipangizo zonse za m'nyumba ya Yehova, zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo anazicotsa muno, kunka nazo ku Babulo;
4 ndipo ndidzabwezeranso kumalo kuno Yekoniya mwana wace wa Yehoyakimu, mfumu ya Yuda, ndi am'nsinga onse a Yuda, amene ananka ku Babulo, ati Yehova: pakuti ndidzatyola gori la mfumu ya ku Babulo.
5 Ndipo Yeremiya mneneri anati kwa Hananiya mneneri pamaso pa ansembe, ndi pamaso pa anthu onse amene anaima m'nyumba ya Yehova,
6 Yeremiya mneneri anati, Amen: Yehova acite cotero: Yehova atsimikize mau ako amene wanenera, abwezerenso zipangizo za nyumba ya Yehova, ndi onse amene anacotsedwa am'nsinga, kucokera ku Babulo kudza kumalo kuno.
7 Koma mumvetu mau awa amene ndinena m'makutu anu, ndi m'makutu a anthu onse:
8 Aneneri amene analipo kale ndisanakhale ine, nimusanakhale inu, ananenera maiko ambiri, ndi maufumu akuru, za nkhondo, ndi za coipa, ndi za caola.