1 Nthawi yomweyo, ati Yehova, ndidzakhala Mulungu wa mabanja onse a Israyeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
2 Atero Yehova, Anthu opulumuka m'lupanga anapeza cisomo m'cipululu; Israyeli, muja anakapuma.
3 Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi cikondi cosatha; cifukwa cace ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima.
4 Ndidzamangitsanso mudzi wako, ndipo udzamangidwa, iwe namwali wa Israyeli; udzakometsedwanso ndi mangaka, ndipo udzaturukira masewero a iwo akukondwerera.
5 Ndiponso udzalima minda ya mphesa pa mapiri a Samariya; akunka adzanka, nadzayesa zipatso zace zosapatulidwa.
6 Pakuti lidzafika tsiku, limene alonda a pa mapiri a Efraimu adzapfuula, Ukani inu, tikwere ku Ziyoni kwa Yehova Mulungu wathu.