8 Ansembe sanati, Ali kuti Yehova? ndi iwo amene agwira malamulo sandidziwa Ine; ndi abusa omwe anandilakwira Ine, ndi aneneri ananenera mwa Baala, natsata zinthu zosapindula.
9 Cifukwa cace ndidzatsutsananso nanu, ati Yehova, ndi ana a ana anu ndidzatsutsana nao.
10 Pakuti pitani ku zisumbu za Kitimu nimuone; tumizani ku Kedara nimulingalire bwino; nimuone ngati cinalipo cotere.
11 Kodi mtundu wa anthu unasintha milungu yao, imene siiri milungu? Koma anthu anga anasintha ulemerero wao ndi cosapindula.
12 Muzizwe pamenepo, miyamba inu, muope kwambiri, mukhale ouma, ati Yehova.
13 Pakuti anthu anga anacita zoipa ziwiri; anandisiya Ine kasupe wa madzi amoyo, nadziboolera zitsime, zitsime zong'aluka, zosakhalamo madzi.
14 Kodi Israyeli ndi mtumiki? kodi ndiye kapolo wobadwa m'nyumba? afunkhidwa bwanji?