13 Ndipo namwali adzasangalala m'masewero, ndi anyamata ndi nkhalamba pamodzi; pakuti ndidzasandutsa kulira kwao kukhale kukondwera, ndipo ndidzatonthoza mitima yao, ndi kuwasangalatsa iwo asiye cisoni cao.
14 Ndipo ndikhutitsa moyo wa ansembe ndi mafuta, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zokoma zanga, ati Yehova.
15 Atero Yehova: Mau amveka m'Rama, maliro ndi kulira kwakuwawa, Rakeli alinkulirira ana ace; akana kutonthozedwa mtima pa ana ace, cifukwa palibe iwo.
16 Yehova atero: Letsa mau ako asalire, ndi maso anu asagwe misozi; pakuti nchito yako idzalandira mphoto, ati Yehova; ndipo adzabweranso kucokera ku dziko la mdani.
17 Ndipo ciripo ciyembekezero ca citsirizo cako, ati Yehova; ndipo ana ako adzafikanso ku malire ao.
18 Kumva ndamva Efraimu alinkulirira kotero, Mwandilanga ine, ndipo ndalangidwa, monga mwana wa ng'ombe wosazolowera gori; munditembenuze ine, ndipo ine ndidzatembenuka; pakuti inu ndinu Yehova Mulungu wanga.
19 Pakuti nditatembenuka, ndinalapa; nditalangizidwa, ndinamenya pa ncafu yanga; ndinakhala ndi manyazi, inde, ndinapepulidwa, cifukwa ndinasenza citonzo ca ubwana wanga.