21 Taimitsa zizindikiro, udzipangire zosonyeza; taika mtima wako kuyang'anira mseu wounda, njira imene unapitamo; tatembenukanso, iwe namwali wa Israyeli, tatembenukiranso ku midzi yako iyi.
22 Udzayenda kwina ndi kwina masiku angati; iwe mwana wamkazi wobwerera m'mbuyo? pakuti Yehova walenga catsopano m'dziko lapansi: mkazi adzasanduka mphongo.
23 Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, Kawirinso adzanena mau awa m'dziko la Yuda ndi m'midzi yace, pamene ndibwezanso undende wao; Yehova akudalitse iwe, wokhalamo cilungamo, iwe phiri lopatulika.
24 Ndipo Yuda ndi midzi yace yonse adzakhalamo pamodzi; alimi, ndi okusa zoweta.
25 Pakuti ndakhutidwa mtima wolema, ndadzazanso mtima uli wonse wacisoni.
26 Pamenepo ndinauka, ndinaona; ndipo tulo tanga tinandizunira ine.
27 Taonani, masiku adza, ati Yehova, amene ndidzafesera nyumba ya Israyeli ndi nyumba ya Yuda ndi mbeu ya anthu ndi mbeu ya nyama.