5 Ndiponso udzalima minda ya mphesa pa mapiri a Samariya; akunka adzanka, nadzayesa zipatso zace zosapatulidwa.
6 Pakuti lidzafika tsiku, limene alonda a pa mapiri a Efraimu adzapfuula, Ukani inu, tikwere ku Ziyoni kwa Yehova Mulungu wathu.
7 Pakuti Yehova atero, Yimbirirani Yakobo ndi kukondwa, pfuulirani mtundu woposawo; lalikirani, yamikirani, ndi kuti, Yehova, mupulumutse anthu anu, ndi otsala a Israyeli,
8 Taonani, ndidzatenga iwo ku dziko la kumpoto, ndidzasonkhanitsa iwo ku malekezero a dziko lapansi, pamodzi ndi osaona ndi opunduka mwendo, mkazi amene ali ndi pakati ndi mkazi alinkubala pamodzi; khamu lalikuru lidzabwera kuno.
9 Adzadza ndi kulira, ndipo ndidzawatsogolera ndi mapembedzero, ndidzawayendetsa ku mitsinje yamadzi, m'njira yoongoka m'mene sadzapunthwa, pakuti ndiri Atate wace wa Israyeli, ndipo Efraimu ali mwana wanga woyamba.
10 Tamvani mau a Yehova, amitundu inu, lalikirani m'zisumbu zakutari; ndi kuti, Iye amene anabalalitsa Israyeli adzasonkhanitsa, nadzamsunga, monga mbusa acita ndi zoweta zace.
11 Pakuti Yehova wapulumutsa Yakobo, namuombola iye m'dzanja la iye amene anamposa mphamvu,