9 Adzadza ndi kulira, ndipo ndidzawatsogolera ndi mapembedzero, ndidzawayendetsa ku mitsinje yamadzi, m'njira yoongoka m'mene sadzapunthwa, pakuti ndiri Atate wace wa Israyeli, ndipo Efraimu ali mwana wanga woyamba.
10 Tamvani mau a Yehova, amitundu inu, lalikirani m'zisumbu zakutari; ndi kuti, Iye amene anabalalitsa Israyeli adzasonkhanitsa, nadzamsunga, monga mbusa acita ndi zoweta zace.
11 Pakuti Yehova wapulumutsa Yakobo, namuombola iye m'dzanja la iye amene anamposa mphamvu,
12 Ndipo adzadza nadzayimba pa msanje wa Ziyoni, nadzasonkhanira, ku zokoma za Yehova, kutirigu, ndi kuvinyo, ndi mafuta, ndi kwa ana a zoweta zazing'ono ndi zazikuru; ndipo moyo wao udzakhala ngati munda wamicera; ndipo, sadzakhalanso konse ndi cisoni.
13 Ndipo namwali adzasangalala m'masewero, ndi anyamata ndi nkhalamba pamodzi; pakuti ndidzasandutsa kulira kwao kukhale kukondwera, ndipo ndidzatonthoza mitima yao, ndi kuwasangalatsa iwo asiye cisoni cao.
14 Ndipo ndikhutitsa moyo wa ansembe ndi mafuta, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zokoma zanga, ati Yehova.
15 Atero Yehova: Mau amveka m'Rama, maliro ndi kulira kwakuwawa, Rakeli alinkulirira ana ace; akana kutonthozedwa mtima pa ana ace, cifukwa palibe iwo.