1 Ndipo padzaturuka mphukira pa tsinde la Jese, ndi nthambi yoturuka m'mizu yace idzabala zipatso;
2 ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;
3 ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera:
4 koma ndi cilungamo adzaweruza aumphawi, nadzadzudzulira ofatsa a m'dziko moongoka; ndipo adzamenya dziko lapansi ndi cibonga ca kukamwa kwace, nadzapha oipa ndi mpweya wa milomo yace.