Yesaya 17 BL92

Aneneratu za Damasiko ndi Efraimu

1 Katundu wa Damasiko. Taonani, Damasiko wacotsedwa usakhalenso mudzi, ndimo udzangokhala muunda wopasudwa.

2 Midzi ya Aroeri yasiyidwa; idzakhala ya zoweta zogona pansi, opanda woziopsya.

3 Ku Efraimu sikudzakhalanso linga, ngakhale ufumu ku Damasiko, ngakhale otsala kwa Aramu; iwo adzakhala ngati ulemerero wa ana a Israyeli, ati Yehova wamakamu.

4 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti ulemerero wa Yakobo udzakhala wopyapyala, ndi kunenepa kwa thupi lace kudzaonda.

5 Ndipo padzakhala ngati wamasika alikumweta tirigu wosaceka, ndi dzanja lace lirikudula ngala; inde padzakhala ngati pamene wina akunkha ngala m'cigwa ca Refaimu.

6 Koma mudzasiyidwa m'menemo khunkha, monga ngati kugwedeza kwace kwa mtengo waazitona, zipatso ziwiri pena zitatu m'nsonga ya nthambi yosomphoka, zinai pena zisanu m'nthambi za kunthemba, za mtengo wobalitsa, ati Yehova, Mulungu wa Israyeli.

7 Tsiku limenelo munthu adzayang'ana kwa Mlengi wace, ndipo maso ace adzalemekeza Woyera wa Israyeli.

8 Ndipo iye sadzayang'ana pa maguwa a nsembe, nchito ya manja ace, ngakhale kulemekeza cimene anacipanga ndi zala zace, ngakhale zifanizo pena mafano a dzuwa.

9 Tsiku limenelo midzi yace yolimba idzakhala ngati mabwinja a m'nkhalango, ndi a pansonga pa phiri, osiyidwa pamaso pa ana a Israyeli; ndipo padzakhala bwinja.

10 Cifukwa iwe waiwala Mulungu wa cipulumutso cako, sunakumbukira thanthwe la mphamvu zako; cifukwa cace iwe waoka mitengo yokondweretsa, waokapo zipinjiri zacilendo;

11 tsiku lako looka uzingapo mpanda, nuphukitsa mbeu zako m'mawa mwace; mulu wa masika udzaoneka tsiku lakulira ndi la cisoni cothetsa nzeru.

Aneneratu za kufafanizika kwa nkhondo ya Asuri

12 Ha, phokoso la mitundu yambiri ya anthu ambiri, amene apfuula ngati kukukuma kwa nyanja: ndi kuthamanga kwa amitundu, akuthamanga ngati kuthamangakwa madzi amphamvu!

13 Mitundu ya anthu idzathamanga ngati kuthamanga kwa madzi ambirimbiri; koma Iye adzawadzudzula, ndipo iwo adzathawira patari, nadzapitikitsidwa monga mankhusu a pamapiri patsogolo pa mphepo, ndi monga pfumbi lokwetera patsogolo pa mkunthu wa mphepo.

14 Pa nthawi ya madzulo, taonani kuopsya; kusanace, iwo palibe. Ili ndi gawo la iwo amene atifunkha ndi ici ciwagwera omwe alanda zathu.