Yesaya 61 BL92

Alalikira Uthenga Wabwino wa cipulumutso

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwakutsegulidwa kwa m'ndende;

2 ndikalalikire caka cokomera Yehova, ndi tsiku lakubwezera la Mulungu wathu; ndikatonthoze mtima wa onse amene akulira maliro;

3 ndikakonzere iwo amene alira maliro m'Ziyoni, ndi kuwapatsa cobvala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, cobvala ca matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo achedwe mitengo ya cilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

4 Ndipo iwo adzamanga mabwinja akale, nadzamanga pa miunda yakale, nadzakonzanso midzi yopasuka, mabwinja a mibadwo yambiri.

5 Ndipo alendo adzaimirira ndi kudyetsa magulu ako, ndi anthu akunja adzakhala olima ako, ndi kukukonzera minda yamphesa.

6 Koma inu mudzachedwa ansembe a Yehova; anthu adzakuyesani inu atumiki a Mulungu wathu; inu mudzadya cuma ca amitundu, nimudzalowa mu ulemerero wao.

7 M'malo mwa manyazi anu, owirikiza; ndi citonzo iwo adzakondwera ndi gawo lao; cifukwa cace iwo adzakhala naco m'dziko mwao colowa cowirikiza, adzakhala naco cikondwerero cosatha.

8 Pakuti Ine Yehova ndikonda ciweruziro, ndida cifwamba ndi coipa; ndipo ndidzawapatsa mphotho yao m'zoonadi; ndipo ndidzapangana nao pangano losatha.

9 Ndipo ana ao adzadziwidwa mwa amitundu, ndi obadwa ao mwa anthu; onse amene awaona adzawazindikira kuti iwo ndiwo ana amene Yehova wadalitsa.

10 Ndidzakondwa kwambiri mwa Yehova, moyo wanga udzakondwerera mwa Mulungu wanga; pakuti Iye wandibveka ine ndi zobvala za cipulumutso, nandipfunda copfunda ca cilungamo, monga mkwati abvala nduwira, ndi monga mkwatibwi adzikometsa yekha ndi miyala yamtengo.

11 Pakuti monga dziko liphukitsa mphundu zace, ndi monga munda umeretsa zobzalamo, momwemo Ambuye Yehova adzaphukitsa cilungamo ndi matamando pamaso pa amitundu onse.