1 Katundu wa Damasiko. Taonani, Damasiko wacotsedwa usakhalenso mudzi, ndimo udzangokhala muunda wopasudwa.
2 Midzi ya Aroeri yasiyidwa; idzakhala ya zoweta zogona pansi, opanda woziopsya.
3 Ku Efraimu sikudzakhalanso linga, ngakhale ufumu ku Damasiko, ngakhale otsala kwa Aramu; iwo adzakhala ngati ulemerero wa ana a Israyeli, ati Yehova wamakamu.
4 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti ulemerero wa Yakobo udzakhala wopyapyala, ndi kunenepa kwa thupi lace kudzaonda.
5 Ndipo padzakhala ngati wamasika alikumweta tirigu wosaceka, ndi dzanja lace lirikudula ngala; inde padzakhala ngati pamene wina akunkha ngala m'cigwa ca Refaimu.