1 Katundu wa cigwa ca masomphenya.Mwatani kuti mwakwera nonsenu pamacindwi?
2 Iwe amene wadzala ndi zimpfuu, mudzi waphokoso, mudzi wokondwa; ophedwa ako, sanaphedwa ndi lupanga, sanafe m'nkhondo.
3 Olamulira ako onse athawa pamodzi, anamangidwa ndi amauta; opezedwa ako onse anamangidwa pamodzi, nathawira patari.
4 Comweco ndinati, Usandiyang'ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, cifukwa ca kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,