1 Tsiku limenelo adzayimba nyimbo imeneyi m'dziko la Yuda, Ife tiri ndi mudzi wolimba; Iye adzaikacipulumutso cikhale macemba ndi malinga.
2 Tsegulani pazipata, kuti mtundu wolungama, umene ucita zoonadi, ulowemo.
3 Inu mudzasunga mtima wokhazikika mu mtendere weni weni, cifukwa ukukhulupirirani Inu.
4 Khulupirirani Yehova nthawi zamuyaya, pakuti mwa Ambuye Yehova muli thanthwe lacikhalire.
5 Cifukwa Iye watsitsira pansi iwo amene anakhala pamwamba, mudzi wa pamsanje; Iye wautsitsa, wautsitsira pansi; waugwetsa pansi pa pfumbi.
6 Phazi lidzaupondereza pansi; ngakhale mapazi a aumphawi, ndi mapondedwe a osowa.