5 Iwo onse adzakhala ndi manyazi, ndi anthu amene sangapindule nao kanthu, amene sakhala kwa iwo thangata, pena phindu, koma manyazi ndi citonzo.
6 Katundu wa zirombo za kumwera.M'dziko lobvuta ndi lopweteka, kumeneko kucokera mkango waukazi, ndi wamphongo, mphiri, ndi njoka youluka yamoto, iwo anyamula cuma cao pamsana pa aburu, ndi ang'ono zolemera zao pa malinundu a ngamila, kunka kwa anthu amene sadzapindula nao.
7 Pakuti thangata la Aigupto liri lacabe, lopanda pace; cifukwa cace ndamucha wonyada, wokhala cabe.
8 Tsopano pita, ukalembe mauwa pamaso pao pathabwa, nuwalembe m'buku, kuti akakhalebe ku nthawi yam'tsogolo, mboni ya masiku onse.
9 Pakuti ali anthu opanduka, ana onama, ana osafuna kumva cilamulo ca Yehova;
10 amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;
11 cokani inu munjira, patukani m'bande, tiletsereni Woyera wa Israyeli pamaso pathu.