6 Bwerani kwa Iye amene mwampandukira kolimba, ana a Israyeli inu.
7 Pakuti tsiku limenelo iwo adzataya munthu yense mafano ace asiliva, ndi mafano ace agolidi amene manja anu anu anawapanga akucimwitseni inu.
8 Pamenepo Asuri adzagwa ndi lupanga losati la munthu; ndi lupanga losati la anthu lidzammariza iye; ndipo iye adzathawa lupanga, ndi anyamata ace adzalamba.
9 Ndipo mwala wace udzacoka, cifukwa ca mantha, ndi akalonga ace adzaopa mbendera, ati Yehova, amene moto wace uli m'Ziyoni, ndi ng'anjo yace m'Yerusalemu.