4 Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.
5 Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.
6 Pakuti wopusa adzanena zopusa, ndi mtima wace udzacita mphulupulu, kucita zoipitsa, ndi kunena za Yehova molakwira, kusowetsa konse mtima wanjala, ndi kulepheretsa cakumwa ca waludzu.
7 Zipangizonso za womana ziri zoipa; iye apangira ziwembu zakuononga waumphawi ndi mau onama, ngakhale pamene wosowa alankhula zoona.
8 Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.
9 Ukani, akazi inu, amene mulinkukhala phe, mumve mau anga; mu ana akazi osasamalira, cherani makutu pa kulankhula kwanga.
10 Pakutha caka, kudza masiku ena inu mudzabvutidwa, inu akazi osasamalira; pakuti masika a mphesa adzasoweka, sadzatuta konse.