9 Musakwiye kopambana, Yehova, musakumbukire zoipa nthawi zonse; taonani, yang'anani ife, tikupembedzani Inu, ife tonse tiri anthu anu.
10 Midzi yanu yopatulika yasanduka cipululu, Ziyoni wasanduka cipululu, Yerusalemu wasanduka bwinja.
11 Nyumba yathu yopatulika ndi yokongola, m'mene makolo athu anakutamandani Inu, yatenthedwa ndi moto; ndi zinthu zathu zonse zokondweretsa zapasuka.
12 Kodi mudzadziletsa pa zinthuzi, Yehova? Kodi Inu mudzakhala cete ndi kutibvutitsa ife zolimba?