12 Cifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;
13 ndi pa mitengo yonse yamkungudza ya Lebano, yaitari ndi yotukulidwa, ndi pa mitengo yonse yathundu ya Basana;
14 ndi pa mapiri onse atari, ndi pa zitunda zonse zotukulidwa;
15 ndi pa nsanja zazitari zonse, ndi pa macemba onse;
16 ndi pa ngalawa zonse za Tarisi, ndi pa zithunzithunzi zonse zokondweretsa.
17 Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.
18 Ndimo mafano adzapita psiti.