9 Munthu wacabe agwada pansi, ndi munthu wamkuru adzicepetsa, koma musawakhululukire.
10 Lowa m'phanga, bisala m'pfumbi, kucokera pa kuopsya kwa Yehova, ndi pa ulemerero wacifumu wace.
11 Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.
12 Cifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;
13 ndi pa mitengo yonse yamkungudza ya Lebano, yaitari ndi yotukulidwa, ndi pa mitengo yonse yathundu ya Basana;
14 ndi pa mapiri onse atari, ndi pa zitunda zonse zotukulidwa;
15 ndi pa nsanja zazitari zonse, ndi pa macemba onse;