3 Ndi pa nyanja zazikuru anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku Nile; ndi kumeneko kunali msika wa amitundu.
4 Khala ndi manyazi, iwe Zidoni; cifukwa nyanja yanena, linga la kunyanja, ndi kuti, Ine sindinamve zowawa, kapena kubala, kapena kulera anyamata, kapena kulera anamwali.
5 Pofika mbiriyo ku Aigupto, iwo adzamva kuwawa kwambiri pa mbiri ya Turo.
6 Olokani inu, kunka ku Tarisi, kuwani, inu okhala m'cisumbu.
7 Kodi umene ndi mudzi wanu wokondwa, wacikhalire kale lomwe, umene mapazi ace anaunyamula kunka nao kutari kukhalako?
8 Ndani wapanga uphungu uno pa Turo, mudzi umene upereka akorona, amalonda ace ali akalonga, ogulitsa ace ali olemekezeka pa dziko lapansi?
9 Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m'dziko lapansi.