1 Tsoka okhulupirira Aigupto. Tsoka kwa ana opanduka, ati Yehova, amene atenga uphungu koma si pa Ine; napangana pangano opanda mzimu wanga, kuti aonjezere cimo ndi cimo;
2 amene ayenda kutsikira ku Aigupto, osafunsa kukamwa kwanga, kudzilimbitsa iwo okha ndi li mphamvu za Farao, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto
3 Cifukwa cace mphamvu za Farao zidzakhala kwa inu manyazi, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto kudzakhala cisokonezo canu.
4 Pakuti akalonga ace ali pa Zaani, ndi mithenga yace yafika ku Hanesi.
5 Iwo onse adzakhala ndi manyazi, ndi anthu amene sangapindule nao kanthu, amene sakhala kwa iwo thangata, pena phindu, koma manyazi ndi citonzo.