4 Ndipo iye anati, Kodi iwo anaona ciani m'nyumba mwanu? Ndipo Hezekiya anayankha, Zonse za m'nyumba mwanga iwo anaziona; palibe kanthu ka mwa cuma canga, kamene ine sindinawaonetse.
5 Ndipo Yesaya anati kwa Hezekiya, Imvani mau a Yehova wa makamu.
6 Taona, masiku afika, kuti zonse za m'nyumba mwako, ndi zimene atate ako anazikundika kufikira lero lino, zidzatengedwa kunka ku Babulo; sipadzatsala kanthu, ati Yehova.
7 Ndipo ana ako amene adzabadwa ndi iwe, amene udzabala, iwo adzawatenga, ndipo adzakhala adindo m'cinyumba cace ca mfumu ya ku Babulo.
8 Ndipo Hezekiya anati kwa Yesaya, Mau a Yehova, amene iwe wanena, ali abwino. Iye anatinso, Pakuti padzakhala mtendere ndi zoonadi masiku anga.