13 Inde ciyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira nchito, ndipo ndani adzaletsa?
14 Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israyeli: Cifukwa ca inu ndatumiza ku Babulo, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Akasidi m'ngalawa za kukondwa kwao.
15 Ine ndine Yehova Woyera wanu, Mlengi wa Israyeli, Mfumu yanu,
16 Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu;
17 amene aturutsa gareta ndi ka valo, nkhondo ndi mphamvu; iwo agona pansi pamodzi sadzaukai; iwo atha, azimidwa ngati lawi.
18 Musakumbukire zidapitazo, ngakhale kulingalira zinthu zakale.
19 Taonani, ine ndidzacita cinthu catsopano; tsopano cidzaoneka; kodi simudzacidziwa? Ndidzakonzadi njira m'cipululu, ndi mitsinje m'zidalala.