22 Atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakodola anthu a mitundu, ndi kukwezera anthu mbendera yanga; ndipo adzabwera nao ana ako amuna pa cifuwa cao, ndi ana ako akazi adzatengedwa pa mapewa ao.
23 Ndipo mafumu adzakulera, ndi akazi ao akuru adzakuyamwitsa; iwo adzakugwadira ndi nkhope zao zoyang'ana pansi, nadzaseteka pfumbi la m'mapazi ako: ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndi iwo amene alindira Ine sadzakhala ndi manyazi.
24 Kodi cofunkha cingalandidwe kwa wamphamvu, pena am'nsinga a woopsya angapulumutsidwe?
25 Koma atero Yehova, Ngakhale am'nsinga a wamphamvu adzalandidwa, ndi cofunkha ca woopsya cidzapulumutsidwa; pakuti Ine ndidzakangana naye amene akangana ndi iwe, ndipo ndidzapulumutsa ana ako.
26 Ndipo ndidzadyetsa iwo amene atsendereza iwe ndi nyama yao yao; ndi mwazi wao wao; iwo adzaledzera monga ndi vinyo wotsekemera; anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndiri Mpulumutsi wako, ndi Mombolo wako, Wamphamvu wa Yakobo.