10 Panganani upo, koma udzakhala cabe; nenani mau, koma sadzacitika; pakuti Mulungu ali pamodzi ndi ife.
11 Pakuti Yehova watero kwa ine ndi dzanja lolimba, nandilangiza ine kuti ndisayende m'njira ya anthu awa, nati,
12 Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.
13 Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.
14 Ndipo Iye adzakhala malo opatulika; koma mwala wopunthwitsa, ndi thanthwe lolakwitsa la nyumba zonse ziwiri za Israyeli, khwekhwe ndi msampha wa okhala m'Yerusalemu.
15 Ndipo ambiri adzapunthwapo, nagwa, natyoka, nakodwa, natengedwa.
16 Manga umboni, mata cizindikilo pacilamulo mwa aphunzi anga.