25 Ine, Inedi, ndine amene ndifafaniza zolakwa zako, cifukwa ca Ine mwini; ndipo Ine sindidzakumbukira macimo ako.
26 Undikumbutse Ine; tiyeni, tinenane pamodzi; fotokoza mlandu wako, kuti ukalungamitsidwe.
27 Atate wako woyamba anacimwa, ndi otanthauzira ako andilakwira Ine.
28 Cifukwa cace ndidzaipitsa akuru a kacisi, ndipo ndidzasanduliza Yakobo akhale temberero, ndi Israyeli akhale citonzo.