1 Cifukwa ca Ziyoni sindidzakhala cete, ndi cifukwa ca Yerusalemu sindidzapuma, kufikira cilungamo cace cidzaturuka monga kuyera, ndi cipulumutso cace monga nyali yoyaka.
2 Ndipo amitundu adzaona cilungamo cako, ndi mafumu onse ulemerero wako; ndipo udzachedwa dzina latsopano, limene m'kamwa mwa Yehova mudzachula.
3 Iwe udzakhalanso korona wokongola m'dzanja la Yehova, korona wacifumu m'dzanja la Mulungu wako.
4 Iwe sudzachedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzachedwanso Bwinja; koma iwe udzachedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.
5 Pakuti monga mnyamata akwatira namwali, momwemo ana ako amuna adzakukwama iwe; ndi monga mkwati akondwera ndi mkwatibwi, momwemo Mulungu wako adzakondwera nawe.
6 Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala cete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale cete,
7 ndipo musamlole akhale cete, kufikira Iye atakhazikitsa naika Yerusalemu akhale tamando m'dziko lapansi.