11 Yehova, dzanja lanu litukulidwa, koma iwo saona; koma iwo adzaona cangu canu ca kwa anthu, nadzakhala ndi manyazi; inde moto udzamariza adani anu.
12 Yehova, udzatikhazikitsira mtendere; pakuti mwatigwirira nchito zathu zonse.
13 Yehova Mulungu wathu, pamodzi ndi Inu ambuye ena adatilamulira ife; koma mwa Inu nokha tidzachula dzina lanu.
14 Iwo afa, atha, sadzakhalanso ndi moyo; ali mizimu, sadzauka; cifukwa cace Inu munawazonda, ndi kuwaononga, mwathetsa cikumbukiro cao conse.
15 Mwacurukitsa mtundu, Yehova, mwacurukitsa mtundu; Inu mwalemekezeka, mwakuza malire onse a dziko.
16 Yehova, iwo adza kwa Inu mobvutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.
17 Monga ngati mkazi wokhala ndi pakati, amene nthawi yace yakubala yayandikira, amva zopweteka, ndi kupfuula m'zowawa zace; momwemo takhala ife pamaso panu, Yehova.