17 Ndipo kuwala kwa Israyeli kudzakhala moto, ndi Woyera wace adzakhala lawi; ndipo lidzatentha ndi kuthetsa minga yace ndi lunguzi wace tsiku limodzi.
18 Ndipo adzanyeketsa ulemerero wa m'nkhalango yace, ndi wa m'munda wace wopatsa bwino, moyo ndi thupi; ndipo padzakhala monga ngati pokomoka wonyamula mbendera.
19 Ndipo mitengo yotsala ya m'nkhalango yace idzakhala yowerengeka, kuti mwana ailembera.
20 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti otsala a Israyeli, ndi iwo amene anapulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzatsamiranso iye amene anawamenya; koma adzatsamira Yehova Woyera wa Israyeli, ntheradi.
21 Otsala adzabwera, otsala a Yakobo, kwa Mulungu wamphamvu.
22 Popeza ngakhale anthu anu Israyeli akunga mcenga wa kunyanja, otsala ao okha okha adzabwera; cionongeko catsimikizidwa, cilungamo cace cisefukira.
23 Pakuti Ambuye Yehova wa makamu adzacita cionongeko cotsimikizidwa pakati pa dziko lonse lapansi.