1 Muimiranji patari, Yehova?Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?
2 Podzikuza woipa apsereza waumphawi;Agwe m'ciwembu anapanganaco.
3 Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace,Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.
4 Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira.Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.
5 Mayendedwe ace alimbika nthawi zonse;Maweruzo anu ali pamwamba posaona iye;Adani ace onse awanyodola.
6 Ati mumtima mwace, Sindidzagwedezeka ine;Ku mibadwo mibadwo osagwa m'tsoka ine.
7 M'kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera;Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.