Masalmo 89 BL92

Pangano la Mulungu ndi Davide. Mulungu adzapulumutsa anthu ace

Cilangizo ca Etana M-ezera.

1 Ndidzayimbira zacifundo za Yehova nthawi yonse:Pakamwa panga ndidzadziwitsira cikhulupiriko canu ku mibadwo mibadwo.

2 Pakuti ndinati, Cifundo adzacimanga kosaleka;Mudzakhazika cikhulupiriko canu m'Mwamba mweni mweni.

3 Ndinacita cipangano ndi wosankhika wanga,Ndinalumbirira Davide mtumiki wanga:

4 Ndidzakhazika mbeu yako ku nthawi yonse,Ndipo ndidzamanga mpando wacifumu wako ku mibadwo mibadwo.

5 Ndipo kumwamba kudzalemekeza zodabwiza zanu, Yehova;Cikhulupiriko canunso mu msonkhano wa oyera mtima.

6 Pakuti kuli yani kuthambo timlinganize ndi Yehova?Afanana ndi Yehova ndani mwa ana a amphamvu?

7 Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri m'upo wa oyera mtima,Ndiye wocititsa mantha koposa onse akumzinga.

8 Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova?Ndipo cikhulupiriko canu cikuzingani.

9 Inu ndinu wakucita ufumu pa kudzikuza kwa nyanja;Pakuuka mafunde ace muwacititsa bata.

10 Mudathyola Rahabu, monga munthu wophedwa;Munabalalitsa adani anu ndi mkono wa mphamvu yanu.

11 Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu;Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.

12 Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.

13 Muli nao mkono wanu wolimba;M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

14 Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu;Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.

15 Odala anthu odziwa liu la lipenga;Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

16 Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse;Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.

17 Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao;Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.

18 Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.

19 Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20 Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.

21 Amene dzanja langa lidzakhazikika naye;Inde mkono wanga udzalimbitsa.

22 Mdani sadzamuumira mtima;Ndi mwana wa cisalungamo sadzamzunza.

23 Ndipo ndidzaphwanya omsautsa pamaso pace;Ndidzapandanso odana naye.

24 Koma cikhulupiriko canga ndi cifundo canga zidzakhala naye;Ndipo nyanga yace idzakwezeka m'dzina langa.

25 Ndipo ndidzaika dzanja lace panyanja,Ndi dzanja lamanja lace pamitsinje.

26 Iye adzandichula, ndi kuti, Inu ndinu Atate wanga,Mulungu wanga, ndi thanthwe la cipulumutso canga.

27 Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba,Womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.

28 Ndidzamsungira cifundo canga ku nthawi yonse,Ndipo cipangano canga cidzalimbika pa iye.

29 Ndidzakhalitsanso mbeu yace cikhalire,Ndi mpando wacifumu wace ngati masiku a m'mwamba.

30 Ana ace akataya cilamulo canga,Osayenda m'maweruzo anga:

31 Nakaipsa malembo anga;Osasunga malamulo anga;

32 Pamenepo ndidzazonda zolakwa zao ndi ndodo,Ndi mphulupulu zao ndi mikwingwirima.

33 Koma sindidzamcotsera cifundo canga conse,Ndi cikhulupiriko canga sicidzamsowa.

34 Sindidzaipsa cipangano canga,Kapena kusintha mau oturuka m'milomo yanga.

35 Ndinalumbira kamodzi m'ciyero canga;Sindidzanamizira Davide;

36 Mbeu yace idzakhala ku nthawi yonse,Ndi mpando wacifumu wace ngati dzuwa pamaso panga.

37 Udzakhazikika ngati mwezi ku nthawi yonse,Ndi ngati mboni yokhulupirika kuthambo.

38 Koma Inu munamtaya, nimunamkaniza,Munakwiya naye wodzozedwa wanu.

39 Munakaniza cipangano ca mtumiki wanu;Munaipsa korona wace ndi kumponya pansi,

40 Munapasula maguta ace onse;Munagumula malinga ace.

41 Onse opita panjirapa amfunkhira:Akhala cotonza ca anansi ace.

42 Munakweza dzanja lamanja la iwo omsautsa;Munakondweretsa adani ace onse.

43 Munapinditsa kukamwa kwace kwa lupanga lace,Osamuimika kunkhondo.

44 Munaleketsa kuwala kwace,Ndipo munagwetsa pansi mpando wacifumu wace.

45 Munafupikitsa masiku a mnyamata wace;Munamkuta nao manyazi.

46 Mudzabisala kosatha kufikira liti, Yehova;Ndi kuzaza kwanu kudzatentha ngati moto kufikira liti?

47 Kumbukilani kuti nthawi yanga njapafupi;Munalengeranji ana onse a anthu kwacabe?

48 Munthu ndani amene adzakhalabe ndi moyo, osaona imfa?Amene adzapulumutsa moyo wace ku mphamvu ya manda?

49 Ciri kuti cifundo canu cakale, Ambuye,Munacilumbirira Davide pa cikhulupiriko canu?

50 Kumbukilani, Ambuye, cotonzera atumiki anu;Ndicisenza m'cifuwa mwanga cacokera ku mitundu yonse yaikuru ya anthu;

51 Cimene adani anu, Yehova, atonza naco;Cimene atonzera naco mayendedwe a wodzozedwa wanu.

52 Wodalitsika Yehova ku nthawi yonse,Amen ndi Amen.